Рет қаралды 3,828
29th September was our wedding anniversary.
Ndikupempha nonse okhudzidwa kuti mundithandize kumema kafukufuku wapadera, kuti timve tsatanetsatane wa zomwe zinachitika pa 10 mpakana pa 11 June. #commissionofinquiry
Mai Mary Chilima, amene anali mkazi wa malemu a Saulos Chilima, apempha Amalawi kuwathandizira kuti pakhale kafukufuku wina wapadera pa ngozi ya ndege yomwe idapha amuna awo ndi anthu ena asanu ndi atatu.
Iwo alemba izi pa tsamba lawo la Facebook pomwe lero akukumbukira tsiku lomwe adalowa m'banja ndi a Chilima.
Pempheroli ladza pomwe magulu ena kuphatikizapo CDEDI, Public Affairs Committee komanso chipani cha UTM akhala akupemphanso kuti pakhale kafukufuku wina.
Maguluwa akukhulupilira kuti lipoti la akatswiri aku Germany silingabweretse poyera mayankho ena monga chomwe chidachedwetsa kufufuza ndegeyi itasowa.
Koma m'mbuyomu, nduna yofalitsa nkhani a Moses Kunkuyu idati boma laika chikhulupiliro chake pa akatswiriwa.
Mu chithunzimu, mai Chilima pa malo omwe padachitikira ndege ku nkhalango ya Chikangawa.