Рет қаралды 23,518
A BON KALINDO WAMANGIDWANSO CHIFUKWA CHOPEZEKA NDI MFUTI.
Atafunsidwa kuti apolisi anadziwa bwanji kuti Kalindo ali ndi mfuti.
Kasambara anayankha kuti: " Kalindo anabwera nayo okha mfutiyo pomwe amafuna kuti apasidwe chilolezo".
Khwima Mchizi yemwe akuyimilira Kalindo anafunsa Kasambara kuti pa nthawi imeneyo anawamanga a Kalindo atabwelesa mfuti yo?
Kasambara anauza bwaloli kuti sanamange Kalindo chifukwa anamupatsa mwayi kuti akabweletse zikalata za mfuti wo.
Bwalo loweruza milandu lawuza Kalindo kuti akumuganizira kuti anapezeka ndi mfuti mopanda chilolezo, mu chaka cha 2021.
Boma lidabweletsa m'bwaloli Innocent Kasambara, yemwe ndi wapolisi wakafukufuku.
Kasambara wauza bwaloli kuti akufuna Kalindo akhale mu chitokosi cha apolisi kamba koti mpaka pano , iwo sanawauzebe apolisi komwe anagula kapena kutenga mfutiwo.
Iye anaonjezera kuti apolisi akufuna Kalindo awalondolere komwe anagula mfutiwo.
Atafunsidwa kuti nchifukwa chani akubweletsa nkhaniyi pano, Kasambara ati kuyambira chaka cha 2021, a Kalindo akhala asakuonetsa chidwi chobweletsa mfutiwo.